Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Akorinto 10:9 - Buku Lopatulika

Kapena tisayese Ambuye, monga ena a iwo anayesa, naonongeka ndi njoka zija.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Kapena tisayese Ambuye, monga ena a iwo anayesa, naonongeka ndi njoka zija.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tisapute Ambuye monga momwe adaaŵaputira ena mwa iwo: paja anthuwo adaphedwa ndi njoka.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tisamuyese Khristu, monga ena mwa iwo anachitira ndipo anaphedwa ndi njoka.

Onani mutuwo



1 Akorinto 10:9
11 Mawu Ofanana  

Popeza analakalakatu kuchidikhako, nayesa Mulungu m'chipululu.


Ndipo anayesa Mulungu mumtima mwao ndi kupempha chakudya monga mwa kulakalaka kwao.


Koma anamuyesa napikisana ndi Mulungu Wam'mwambamwamba, osasunga mboni zake;


Pamene makolo anu anandisuntha, anandiyesa, anapenyanso chochita Ine.


Pamenepo anthu anatsutsana ndi Mose, nati, Tipatseni madzi timwe. Koma Mose ananena nao, Mutsutsana nane bwanji? Muyeseranji Yehova?


Ndipo anatcha dzina la malowo Masa, ndi Meriba, chifukwa cha kutsutsana kwa ana a Israele; popezanso anayesa Yehova, ndi kuti, Kodi Yehova ali pakati pa ife, kapena iai?


Musamayesa Yehova Mulungu wanu, monga munamyesa mu Masa.