Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Akorinto 10:5 - Buku Lopatulika

Koma ochuluka a iwo Mulungu sanakondwere nao; pakuti anamwazika m'chipululu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma ochuluka a iwo Mulungu sanakondwera nao; pakuti anamwazika m'chipululu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Komabe ambirimbiri mwa iwo Mulungu sadakondwere nawo, kotero kuti adafera m'chipululu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ngakhale zinali choncho, Mulungu sanakondwere ndi ambiri a iwo, motero ambiri mwa iwo anafera mʼchipululu.

Onani mutuwo



1 Akorinto 10:5
16 Mawu Ofanana  

Potero anawasamulira dzanja lake, kuti awagwetse m'chipululu:


Ambuye, Inu munatikhalira mokhalamo m'mibadwomibadwo.


Chifukwa chake ndinalumbira mu mkwiyo wanga, ngati adzalowa mpumulo wanga.


Monga ndinaweruza makolo anu m'chipululu cha dziko la Ejipito, momwemo ndidzaweruza inu, ati Ambuye Yehova.


popeza anthu onse awa amene adaona ulemerero wanga, ndi zizindikiro zanga, ndidazichita mu Ejipito ndi m'chipululu, koma anandiyesa Ine kakhumi aka, osamvera mau anga;


amuna amene anaipsa mbiri ya dziko, anafa ndi mliri pamaso pa Yehova.


Ndipo masiku amene tinayenda kuchokera ku Kadesi-Baranea, kufikira tidaoloka mtsinje wa Zeredi, ndiwo zaka makumi atatu mphambu zisanu ndi zitatu; kufikira utatha mbadwo wonse wa amuna ankhondo m'chigono, monga Yehova adawalumbirira.


Koma anakwiya ndi ayani zaka makumi anai? Kodi si ndi awo adachimwawo, amene matupi ao adagwa m'chipululu?


Koma ndifuna kukukumbutsani mungakhale munadziwa zonse kale, kuti Ambuye, atapulumutsa mtundu wa anthu ndi kuwatulutsa m'dziko la Ejipito, anaononganso iwo osakhulupirira.