Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




1 Akorinto 10:15 - Buku Lopatulika

Ndinena monga kwa anzeru; lingirirani inu chimene ndinena.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndinena monga kwa anzeru; lingirirani inu chimene ndinena.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndikulankhula nanu ngati anthu anzeru. Muweruze nokha zimene ndikunenazi.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndikuyankhula kwa a anthu anzeru zawo, nokha muweruze pa zimene ndikunenazi.

Onani mutuwo



1 Akorinto 10:15
9 Mawu Ofanana  

Chifukwa chake, okondedwa anga, thawani kupembedza mafano.


Chikho cha dalitso chimene tidalitsa, sichili chiyanjano cha mwazi wa Khristu kodi? Mkate umene tinyema suli chiyanjano cha thupi la Khristu kodi?


Lingirirani mwa inu nokha: Kodi nkuyenera kuti apemphere kwa Mulungu, wosafunda mutu?


Abale, musakhale ana m'chidziwitso, koma m'choipa khalani makanda, koma m'chidziwitso akulu misinkhu.


Tili opusa ife chifukwa cha Khristu, koma muli ochenjera inu mwa Khristu; tili ife ofooka, koma inu amphamvu; inu ndinu olemekezeka, koma ife ndife onyozeka.


Ndinena ichi kukuchititsani inu manyazi. Kodi nkutero kuti mwa inu palibe mmodzi wanzeru, amene adzakhoza kuweruza pa abale,


Koma za zoperekedwa nsembe kwa mafano: Tidziwa kuti tili nacho chidziwitso tonse. Chidziwitso chitukumula, koma chikondi chimangirira.


Yesani zonse; sungani chokomacho,