Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 67 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 67

Amitundu alemekeze Mulungu
Kwa Mkulu wa Nyimbo, pa Neginoto. Salimo. Nyimbo.

1 Atichitire chifundo Mulungu, ndi kutidalitsa, atiwalitsire nkhope yake;

2 kuti njira yanu idziwike padziko lapansi, chipulumutso chanu mwa amitundu onse.

3 Anthu akuyamikeni, Mulungu; anthu onse akuyamikeni.

4 Anthu akondwere, nafuule mokondwera; pakuti mudzaweruza anthu molunjika, ndipo mudzalangiza anthu padziko lapansi.

5 Anthu akuyamikeni, Mulungu; anthu onse akuyamikeni.

6 Dziko lapansi lapereka zipatso zake, Mulungu, Mulungu wathu adzatidalitsa.

7 Mulungu adzatidalitsa; ndipo malekezero onse a dziko lapansi adzamuopa Iye.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi