Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa

Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano


Masalimo 123 - Buku Lopatulika Buku Lopatulika
Masalimo 123

Pemphero la wonyozedwa
Nyimbo yokwerera.

1 Ndikweza maso anga kwa Inu, kwa Inu wakukhala kumwamba.

2 Taonani, monga maso a anyamata ayang'anira dzanja la ambuye wao, monga maso a adzakazi ayang'anira dzanja la mbuye wao wamkazi: Momwemo maso athu ayang'anira Yehova Mulungu wathu, kufikira atichitira chifundo.

3 Mutichitire chifundo, Yehova, mutichitire chifundo; pakuti takhuta kwambiri ndi mnyozo.

4 Moyo wathu wakhuta ndithu ndi kuseka kwa iwo osasowa kanthu, ndi mnyozo wa odzikuza.

Bible Society of Malawi

Bible Society of Malawi