9 Ndipulumuseni, imwe Chawuta kwaazondi wangu! Nin'thawila kwayimwe kuzabisala!
Ninilila kwayimwe, imwe Chawuta ndiniti; imwe ndimwe pakupotela pangu, chigawo changu mudziko lawanthu wamoyo.
Ndibuliseni muchitokisi, kuti nditende dzina lanu! Wakulungama an'zandizungunuka; pakuti mun'zandichitila bzizinji.
M'manja mwanu, ndimo muna nthawe zanu, ndipulumuseni kuchoka m'manja mwaazondi wangu, pomwe naawo anin'thamangisa!
Pantsiku yandichachemelela kwayimwe, azondi wangu an'zachungunuka achibwezewa mbuyo. Ichi nin'dziwa, Mulungu anayine.
Ninilila kwayimwe Mulungu Nyakudzulu-dzulu, kwa Mulungu anim'bwezelela.
Mulungu wangu, ndipulumuseni kwaazondi wangu! Ndilomboleni kwaawo anim'mukila!