4 Nakutenepo n'zimu wangu um'mala mphamvu mwayine, ntima wangu ukubva mantha nkati mwangu.
Imwe Chawuta, ibvani pemphelo langu! Lekani kulila kwangu kufike kwayimwe!
pamwepo madzi yakhadatigwanila, kukukuma kwamadzi kukhadatinyuza;
N'zimu wangu pawum'mala mphamvu, imwe mun'dziwa njila yangu! Munjila yaninfamba, adanditeya ukhukha.
Nin'nyangana kujanja ladidi ndichiwona, koma palibe anin'dziwa; palibe mbuto yakuthawila, palibe munthu aniniwonambo.
Chewukani kwayine, mundikomele ntima, pakuti ndili ndekha pomwe ndikuwawiwa!
Ndaphatiwa namantha, ndikutotetemela, ngozi idamugwanila.
Ndili kudamalila dziko, nin'chemela kwayimwe, ntima wangu pawuninga wafoka; nditsogoleleni kumwala utali kupita ine!
Ninkumbukila, Mulungu nim'buwula, paninilingilila, n'zimu wangu um'mala mphamvu. Selah.
Ninti, nin'zakumbukila nyimbo yangu usiku, nin'zalingilila ndichipsaga-psaga n'zimu wangu.